Top Latest News & Reports

KWANU N'KWANU
04 Feb 2025

KWANU N'KWANU

...Boma la Mozambique Lapempha Mzika Zake Kuti Zibwelere Kwawo.

Boma la Mozambique lapempha mzika zake zomwe zidathawa zipolowe zokhudza chisankho ndipo zikukhala m'dziko muno kuti zibwelere kwawo.

Mtsogoleri wa Nthambi Yoona za Ngozi Zogwa Mwadzidzidzi Mai Luisa Celma Meque apereka pempholi Lachisanu (pa 31 January) pa kampu ya Nyamithuthu m'boma la Nsanje pomwe anakayendera zina mwa mzika zoposa 7,000 zomwe zili pa kampuyi.

"Sichapafupi kuti dziko lidzisamalira mzika za dziko lina mwachikondi ngati mmene ziliri kuno. Mmalo mwa President Chapo, ndikuthokoza mmene Boma la Malawi linakulandilirani komanso mmene likukusamalirani. Izi zikusonyeza ubale wabwino pakati pa maiko athu.

"Ngakhale izi zili chonchi, dziwani kuti zipolowe zinatha m'dziko lathu ndipo muli bata. Tiyeni tibwelere kwathu," anatero a Meque uku anthu akufuula mokondwera.

Mai Meque, omwe anafika m'dziko muno dzulo kudzera ku chipata cha Mwanza pa mdipiti omwe panalinso galimoto zikuluzikulu zitatu zomwe zinanyamula katundu monga mpunga, mchere, ufa ndi mabulangete, ati akabwelera kwawo akakonza ndondomeko yoti anthuwo abwelere kwawo.

Padakali pano, a Meque ndi mdipiti wawo abwelera ku Mozambique kudzera pa chipata cha Mwanza.

 

Visitors Counter

1145535
Today
Yesterday
This Week
Last Week
This Month
Last Month
All days
488
1319
3266
1135414
15835
40171
1145535

Your IP: 3.133.79.80
2025-04-15 13:57

OUR CONTACTS

Department of Disaster Management Affairs

P/Bag 336

Capital City

Lilongwe3

MALAWI.

E-Mail: info.dodma@dodma.gov.mw

Tel:    +265 (0)1 788 188

Fax:   +265 (0)1 789 142

MEDIA AND PUBLIC RELATIONS

For more information on department's media and Public Relations please contact our Public Realations Officer CHIPILIRO KHAMULA